Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mutharika Wati Boma Lake Silatsankho

$
0
0

Mtsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika  wati sizowona zomwe anthu ena akumanena zoti  boma lake limapanga tsankho posankha anthu m'maudindo.

Mutharika amayankhula izi lamulungu pamsonkhano omwe anachititsa pa sukulu yapulaimale ya Nyambadwe mumzinda wa Blantyre.

Iye wati boma lake likuyesetsa kumayika anthu mmaudindo poyang’anira zoyenereza zomwe ali nazo.

Pamenepa pulezidenti Mutharika anapereka zitsanzo za akuluakulu monga mkulu wazamalamulo yemwe amachokera mchigawo chakumpoto, mkulu wa asilikali yemwe ndi wamdera lakumvuma ndinso ena ambiri.

Mwazina pamsonkhanowu Pulezidenti Mutharika analongosolanso zina mwa zitukuko zomwe boma lake lakwaniritsa monga  kuchepetsa chiwerengero cha nduna za boma komanso  kumanga sukulu zophunzitsa ntchito zamanja zam'madela.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875