Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mayi Banda ndi Okhudzidwa ndi Imfa ya a Nyondo

$
0
0

Pamene atsogoleri osiyanasiyana pandale akupitiliza kusonyeza kukhudzidwa kwawo ndi imfa ya mtsogoleri  wachipani cha National Salvation Front NASAF a James Nyondo, mtsogoleri wakale wa dziko lino mayi Joyce Banda ati dziko lino lataya munthu ofunikira kwambiri.

A James Nyondo amwalira lachisanu kuchipatala cha Steve Biko Academic mdziko la South Africa atadwala matenda a khansa ya mmapapu.

Chikalata chomwe akuofesi ya mtsogoleri wakaleyu atulutsa lamulungu chati malemu Nyondo anali munthu wa masomphenya aakulu pa zatsogolo la dziko lino, ndipo asadamwalire wakhala akukambirana naye nkhani zosiyanasiyana zokhudza chitukuko.

Padakali pano akubanja la Nyondo akukonza zobweretsa thupi la malemuwa mdziko muno.

A James Nyondo adayamba kupikisana nawo pa mpando wa pulezidenti ngati mtsogoleri oyima payekha mchaka cha 2009, ndipo adayimanso paudindowu pachisankho cha pa 20 May 2014.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>