Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anthu 40 Afa pa Nyanja ya Mediterranean

$
0
0

Anthu pafupifupi makumi anayi amila mu nyanja ya Mediterranean mdera lina lomwe lili kufupi ndi dziko la Libya bwato lomwe anakwera litamila.

Panthawiyi anthuwo ati anali paulendo opita mmayiko akuulaya pothawa umphawi mmayiko awo.

Anthu makumi asanu ndi anayi mwa anthuwo ati apulumutsidwa, ndipo padakali pano afika mdziko la Italy.

Bungwe la mgwirizano wa mayiko padziko lonse la United Nations lati anthu oposa zikwi makumi asanu ndi imodzi 60 sauzande ndi omwe apezeka akuthawa mmayiko awo kamba ka umphawi chaka chino chokha kuchokera kunsi kwa chipululu cha Sahara.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>