Mtsogoleri wa dziko la Nigeria Muhammadu Buhari lachitatu akuyembekezeka kukakumana ndi mtsogoleri wa dziko la Cameroon a Paul Biya kuti akakambirane mfundo zofuna kuthetsa gulu la zauchifwamba la Boko Haram.
Malipoti a News 24 ati chimukhazikitsire pa udindowu Pulezidentiyu wayenderapo kale mayiko a Chad ndi Niger omwe ndi oyandikana ndi dzikoli pofuna kupeza njira zothanira ndi gululi.
Anthu zikwizikwi mmayikowa akhala akuchitiridwa ziwembu ndi gululi kamba kofuna kukhazikitsa ulamuliro wa chisilamu mdziko la Nigeria.