Apolisi m’boma la Dowa amanga mzika zisanu ndi zinayi za mdziko la Ethiopia zomwe zalowa mdziko muno popanda zitupa zoyenera.
Apolisi m’bomalo agwira anthuwa usiku wa lamulungu lapitali atawapeza akuchokera patchire lina pomwe anabisala podikilira nthawi kuti akalowe kumalo a anthu othawa kwawo m’bomalo a Dzaleka.
Malinga ndi ofalitsa nkhani za apolisi m’bomali Sergeant Richard Kaponda anthuwa omwe ndi a zaka zapakati pa 16 ndi 26 awuza apolisi kuti pa nthawiyi anali paulendo opita mdziko la South Africa pothawa umphawi mmayiko awo.
Anthuwa akuyembekezeka kukawonekera kubwalo loyamba lamilandu m’bomalo komwe akayankhe mulandu olowa mdziko muno popanda zitupa zowayenereza.