Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anthu Awiri Afa ndipo Ena 9 Avulala pa Ngozi ya Galimoto M’boma la Zomba

$
0
0

Anthu awiri afa ndipo ena asanu ndi anayi avulala minibus yomwe anakwera itagubuduzika  dalaivala wake atalephera kuwongolera m’boma la Zomba.

 

Wofalitsa nkhani za apolisi m’bomali a Patricio Supriano watsimikiza za nkhaniyi.

 

Iwo ati minibus-yo yomwe ndi ya mtundu wa Toyota Hiace nambala yake ndi BS 8345 amayendetsa ndi a Willy Kapinga, ndipo yagubuduzika teyala lake litaphulika zomwe zinachititsa kuti alephere kuwongolera moyenera.

 

Anthu awiriwo amwalira pa malo pomwepo ndipo asanu ndi anayiwo akulandira thandizo ku chipatala chachikulu cha Zomba.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>