Anthu khumi afa ndi ena anayi avulala kodetsa nkhawa ndi moto omwe unabuka mwadzidzi mu nyumba ina mu mzinda wa Paris mdziko la France.
Malinga ndi malipoti a wayilesi ya BBC chomwe chinayambitsa motowo padakali pano sichinadziwike.
Pangoziyi anthu ena ati anakwanitsa kudathawa kudzera mmawindo ndipo motowo ati unakhudza nyumba zina khumi ndi zisanu zoyandikana ndi nyumba yomwe motowo unabuka.
Malipoti ati ngozi ya moto wa mtunduwu nkoyamba kuchitika mdzikolo patapita nthawi yayitali.