Mtsogoleri wa dziko lino Dr Joyce Banda wapempha akhristu kuti akondwelere kuwuka kwa Yesu khristu poika mapemphero patsogolo mu chikondwelero cha Pasaka.
President Joyce Banda walangizanso anthu omwe akukasangalala kutali ndi nyumba zawo kuti awonetsetse kuti katundu wawo ali otetezedwa.
Malinga ndi chikalata chomwe Ofesi yofalitsa nkhani ku nyumba ya boma yatulutsa, mtsogoleri wadziko linoyu walangizanso oyendetsa galimoto m'dziko muno kuti ayendetse galimoto mosamala mu nyengoyi popewa ngozi.