Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Matupi a Asilikali Khumi a Mdziko la Uganda Apita Nawo Kwawo

$
0
0

Matupi khumi a asilikali a dziko la Uganda omwe anafa, gulu la zauchifwamba la Al-shabab litachita zamtopola kumalo omwe asilikaliwa amakhaka omwe ali pamtunda wamakilomita 90 kumm’wera chakunzambwe kwa mzinda wa Mogadishu apita nawo m`dziko la Uganda.

 

Malinga ndi malipoti a BBC asilikali khumi ndi awiri a m`dziko la Uganda anaphedwa ndi zigawenga zaAl-shabab  lachiwiri ndipo zigawengazo  zinapha asilikali okwana 70.

 

Omwe anaona izi zikuchitika ati  zigawengazo zinaphulitsa bomba la timkenawo m`galimoto pachipata cholowera pamalowa ndipo kenako zinayamba kuwombera komwe kunatenga ola limodzi.

 

Asilikali a dziko la Uganda ali m`gulu la asikali 22 sauzande  a bungwe la African Union AU omwe pamodzi ndi asilikali a dziko la Uganda akulimbana ndi zigawengazi.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>