Mmodzi wa akuluakulu a chipani cha Alliance For Democracy (AFORD) watsutsa zomwe wayankhula wapampando wachipanichi a Enock Chakufwa Chihana kuti chipani cha AFORD chigwira ntchito ndi cha People’s Party (PP) ponena kuti n’zamutu mwawo osati maganizo a chipanichi.
A Chihana anauza mtundu wa a Malawi kuti chipani chawo chigwira ntchito ndi cha People’s pa 20 April 2013 pa msonkhano wa chipani cha PP omwe unachitikira pa bwalo la zamasewelo la Lumbira ku Chilomoni mu mzinda wa Blantyre.
Pamsonkhanowo A Chihana anati sakuona mtsogoleri aliyense kumbali yotsutsa boma yemwe angachite zinthu ngati mtsogoleri wa dziko lino Dr Joice Banda.
A Msowoya ati izi zikungowonetsa kuti a Chihana siwoyenera kukhala mtsogoleri wachipanichi chifukwa iwo sali ndi chidwi ndi chipani chawo cha AFORD.
“A Chihana akungofuna mpando wa unduna osati kuchita zinthu zokomera chipani cha AFORD n’chifukwa chake abwera poyera kuti akusapota chipani cha Peoples”,atero a Msoyoya.