Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

APOLISI AGWIRA MWAMUNA OPEZEKA NDI MFUTI POPANDA CHILOLEZO

$
0
0

 

A polisi ku Mzuzu agwira ndi kutsekera m'chitolokosi mwamuna wina yemwe amasunga mfuti ziwiri za mtundu wa Green nala m’boma la Karonga .

 Mneneri wa a Polisi ku Mzuzu Sergeant Morris Chapola wati mwamunayo  ndi Bonface Nkhamba  wochokera m’mudzi wa Musenga kwa Mfumu yaikulu Wansambo m’boma la Karonga.

“A Nkhamba anali  m’chitolokosi cha a polisi kale kaamba koti  anapalamulanso milandu ina.  Anthu akufuna kwabwino ndi omwe anatsina khutu apolisi kuti mkuluyo amasunga mfuti kunyumba kwake ku Karonga” atero a Chapola.

Malinga ndi a Chapola a Nkhamba amasunga mfutizo padenga la maudzu la nyumba yawo .

A Bonface Nkhamba akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu posachedwapa ndi kukayankha mlandu wopezeka ndi mfuti popanda chilolezo.
 

 

 

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>