Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bwalo la Milandu Mdziko la SA Lipeza Pulezidenti Zuma Olakwa

$
0
0

Bwalo lalikulu lamindu mdziko la South Africa lagamula kuti mtsogoleri wa dzikolo a Jacob Zuma anaphwanya lamulo polephera kubweza ndalama za boma zomwe anagwiritsa ntchito pochitira chitukuko dera la kwao.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC bwalolo lapereka masiku makumi asanu ndi limodzi  ku nthambi yoona za chuma mdzikolo kuti yiwokhetse ndalama zomwe Pulezident Zuma akuyenera kubweza.

Chigamulocho ati chabweretsa chimwemwe kwa zipani  zotsutsa boma mdzikolo zomwe ati ziyesetsa kuti Pulezidenti Zuma atule pansi udindowu.

Malipoti ati akuluakulu a chipani  cholamula cha African National Congress ANC akhala pansi kuti akambirane za chigamulochi.

Ngakhale pulezidentiyu wagamulidwa, iye akutsutsabe kuti palibe chomwe analakwitsa.

Bwalo lalikulu lamindu mdziko la South Africa lagamula kuti mtsogoleri wa dzikolo a Jacob Zuma anaphwanya lamulo polephera kubweza ndalama za boma zomwe anagwiritsa ntchito pochitira chitukuko dera la kwao.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC bwalolo lapereka masiku makumi asanu ndi limodzi  ku nthambi yoona za chuma mdzikolo kuti yiwokhetse ndalama zomwe Pulezident Zuma akuyenera kubweza.

Chigamulocho ati chabweretsa chimwemwe kwa zipani  zotsutsa boma mdzikolo zomwe ati ziyesetsa kuti Pulezidenti Zuma atule pansi udindowu.

Malipoti ati akuluakulu a chipani  cholamula cha African National Congress ANC akhala pansi kuti akambirane za chigamulochi.

Ngakhale pulezidentiyu wagamulidwa, iye akutsutsabe kuti palibe chomwe analakwitsa.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>