Akhristu alimana la St .Joseph ku St.John Church m'parish ya Kausi mu Diocese ya Mangochi awalimbikitsa za ubwino wopeleka mowolowa manja pa miyambo yonse yochitika mu mpingowu.
Bambo mfumu a parishiyi bambo Kingsley Tebulo ndi omwe anena izi pa mwambo wa misa ya masika pomwe akhristu a limanali amapeleka gawo la zokolora zawo za chaka chino . Iwo ati munthu amene amapereka mowolowa manja amalandira zochuluka kuchokera kwa Mulungu.
↧