Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse, Papa Fransisko, anachita zokambirana ndi atolankhani a nyuzipepala ina ya m’dziko la France komwe mwa zina wakambapo udindo wa mpingo m’maiko a ku Ulaya pa anthu othawa kwao komanso m’mene angadzetsere mgwirizano pakati pa akhristu ndi asilamu.
Papa wati mpingo m’maiko a ku Ulaya sukuyenera kusala anthu othawa kwawo a m’maiko a ku Africa kaamba koti akukumana ndi mavuto a nkhondo, njala komanso kusowa kwa ntchito m’maiko a kwao.
Iye watinso pamene mpingo wakatolika ukuchita chaka chachifundo akhristu komanso asilamu akuyenera kuphunzira kukhalira limodzi komanso kuchitira zinthu ngati ana a banja limodzi.