Mpingo wa katolika m`dziko la Angolawa dzudzula m`chitidwe wa akuluakulu a boma omwe akumalanda malo anthu a kumidzi ndi ku ma kawapeleka kwa anthu a bizinesi .
Malinga ndi wailesi ya Vatican, Episkopi wa dayosizi ya Namibe ya mpingowu ambuyeDionisious Hisilinapo wati anthu akumidzi m`dzikolo akulandidwa malo omwe anasiyilidwa ndi makolo zomwe zikudzetsa mavuto akululu pakati pawo.
Malo omwe anthuwa akulandidwa ati kwambiri akuti ndi omwe amagwilitsa ntchito podyetsera ziweto zawo.