Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Parish Ya St. Anna Ichita M’bindikiro

$
0
0

Parish ya mpingo wakatolika ya  St. Anna ku Kapire    mu dayosizi  ya Mangochi yati imadziwa zakufunika kolimbikitsa moyo wauzimu pakati pa akhristu ake.

Bambo mfumu a parishi-yi bambo Danasio Malajira anena izi pakutha pa mbindikiro umene parishi-yi inakonzera akhristu ake. Mbindikirowu unayamba pa 20 May ndipo watha pa 22 May 2016.

Mbindikirowu wachitika pa mutu wakuti “Chaka Cha Chifundo, Chaka Chopempha Chifundo, Komanso Chaka Chopeleka Chifundo.” Omwe anatsogolera m’bindikirowu ndi Bambo Joseph Kimu omwenso ndi a Director a Radio Maria Malawi.

Bambo Malajira anathokoza akhristu-wa kamba ka chidwi chomwe awonetsa pofika ku mbindikiro-wu mwa unjinji wawo. Iwo ati izi zasonyeza kuti ndi akhristu olimbikira pa chikhulupiliro chawo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>