Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Wati Akhristu Apempherere Mtendere wa Mmaiko Onse

$
0
0

M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Franciskowapempha anthu ndi akhristu a mpingowu kuti lachitatu akumbukire kupemphelera mtendere wa m’mayiko pa dziko lonse.

Malinga ndi malipoti a nyuzipepala ina ya mpingowu, Papa wati wachita izi pomwe mpingowu ukukumbukira kuti patha zaka ziwiri chikhazikitsireni m’gwilizano wa pakati pa atsogoleri a mpingowu ndi a maiko a Israel ndi Palestine opemphelera mtendere m’maiko a Aluya.

Malipoti ati mapemphero a chaka chino, anthu akuyenera kulimbikitsa mapemphero pakati pa anthu omwe akuthawa m’maiko awo kamba kosowa ntchito komanso nkhondo kuti azindikire za chikondi choposera chomwe Mulungu amakhala nacho pakati pawo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>