Dayosizi ya mpingo wakatolika ya Chikhwawa yati iwonetsetsa kuti ntchito za Bungwe lowona zachitukuko mumpingowu la CADECOM zikupindulira anthu onse mu Dayosiziyo.
Episikopi wa Dayosiziyi wolemekezeka Ambuye Peter Musikuwa anena izi pamwambo wokhazikitsa ntchito yothandiza anthu kutukuka pa chuma, umoyo ndinso kudzikonzekeretsa pa ngozi zogwa mwadzidzi.
“kunkhazikitsa kwa pulogaramu imeneyi anthu ambiri osowa chinthandizo alandila chinthandizo mokwanila ,pakutelo tikutukula miyoyo yawo komanso kutukula dziko lanthu.” Anatelo Ambuye Musikuwa.
Iwo anapitiliza ponena kuti mpigo unankhazikisidwa ndi cholinga chakuti munthu yense anthe kutukuka muuzimu ndi muthupi.
Ndipo Paramaunti Tchifi Lundu ya m’bomali inanthokoza bungwe la Cadecom ponkhazikitsa pulogaramuyi.
“Mu pulojekitiyi muli zinthu zingapo monga za Ulimi,jenda, Mabanki komanso za Umoyo, koma kwakukulu ndikunthetsa njala ,ndiye ife tailandila ndi manja awiri.” Anatelo A Lundu.
Ndipo tchitoyi akuyitcha Ubale yomwe idzitsogoleredwa ndi bungwe la CADECOM mu Dayosiziyi.