Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anthu Makumi Atatu Afa Zigawenga za Islamic State Zitaphulitsa Bomba La Timke Nawo

$
0
0

Anthu makumi atatu afa, ndipo ena 80 avulala  gulu la zigawenga la Islamic State litaphulitsa  mabomba awiri atinkenawo  munzinda wa Baghdad  m`dziko la Iraq

Malinga ndi malipoti awailesi ya BBC, bomba loyamba linaphulika m`dera la Shiandipo linapha anthu 19 pomwe bomba lina linaphulika  pamalo ena pomwe asilikali amachitira chipikisheni  a Taji kumpoto kwa mzinda wa Baghdad  ndikupha  anthu  11 kuphatikizapo asilikali.

Gulu la zigawengazi ati likupitiriza kuchita zamtopola  munzindawu pomwe asilikali adzikoli akulimbikitsa  ntchito  yolanda   maziko azigawengazi otchedwa  Falluja  omwe ali pamtunda wa makulomita 60 kumwera kwa mzinda wa Baghdad.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>