Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Polisi ya Kanengo Iyenda Ulendo Wandawala Pofuna Kuzindikiritsa Anthu za Kuipa Kwa Mchitidwe Wopha M

$
0
0

Ngati njira imodzi yotenga  nawo gawo pa ntchito yothana ndi m`chitidwe wopha anthu a mtundu wa chi alubino, apolisi a Kanengomu m’zinda wa Lilongwe akonza  ulendo wa ndawala womwe cholinga chake ndikuzindikiritsa anthu za kuipa kwa m`chitidwe  wopha anthu-wa mdziko muno. 

M’neneri wa apolisi pa polisi ya Kanengo, mai Salome Chibwana, wati apolisi mogwirizana ndi anthu onse ozungulira Kanengo kuphatikiza omwe ndi ma alubino, a mipingo yosiyanasiyana asing’anga komanso azipani zonse za ndale ndiwo atenge mbali pa ulendowu.

Mutu wa ndawala-yi ndi woti “Apolisi sakugwilizana ndi mchitidwe wozembetsa Komanso Kuphedwa Kwa Anthu A Chi Alubino” Ulendowu ukayambira Pa Salima Turn Off kuzungulira Area 25 ku Lilongwe ndi kukamaliza ku polisi ya Kanengo , komwe kukakhale msonkhano womaliza wozindikilitsa anthu za kuyipa kwa mchitidwe-wu m’dziko muno.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>