Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Alshabaab Yapha Asilikali Makumi Anayi a AU ku Somalia

$
0
0

Gulu la zigawenga la  Al-Shabaab  lati lapha   asilikali okwana  makumi anayi  pachiwembu  chomwe linachita  kumalo a asilikali  a African Union   m`chigawo chapakati pa dziko la Somalia.

Bungwe la AUlatsimikiza za chiwembuchi ndipo  anthu omwe azungulira malowa ati anamva kulira kwa mfuti pa malowa. Asilikali abungwe la African Union akuthandiza asilikali adziko la Somalia kulimbana ndi guluri lomwe likulamulira madera osiyanasiyana m`dzikolo.

Dziko la Ethiopia ndi limodzi mwa maiko asanu omwe anatumiza asilikali ake m’dziko la Somaliakukathandiza pa ntchito yothana ndi zigawengadzi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>