Boma la dziko la Iraq lalanda nyumba yake yomwe mumapezeka zigawenga za chisilamu za Islamic State mu mzinda wa Fallujah mdzikolo.
Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC akuluakulu a gulu la zigawengazi achoka m’nyumbayo potsatira kumenyana kwa pakati pa asilikali a boma a dzikolo ndi zigawengazi.
Malipoti ati boma la dzikolo linakhazikitsa kumenyana kwa pakati kwa magulu awiriwa pofuna kulanda mzindawo omwe wakhala uli mmanja mwa zigawengazi kwa nthawi yaitali.