Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bungwe la YODEP Likukhazikitsa Mabungwe Othana ndi Nkhanza kwa Ana ndi Amayi

$
0
0

Bungwe la Youth Development and Productivity (YODEP)m’boma la Zomba  lati ntchito yokhazikitsa ma bungwe a abambo omwe akhale akuteteza amayi ndi ana ku nkhanza zosiyanasiyana ikuyenda bwino.

Mmodzi mwa akuluakulu ku bungweli a Joy Mwandama ndi omwe anena izi polankhula  ndi Radio Maria Malawi.

 Iwo ati padakali pano magulu 77 akhazikitsidwa kale kwa mfumu yaikulu  Mbiza ndi Mwambo ndipo ayamba kale maphunziro.

Maphunzirowa ati athandiza abambo kuti awoneke  mwatsopano pokhala patsogolo kuteteza amayi ndi ana ku nkhanza zomwe zikumakolezera matenda a Edzi.

Ntchitoyi akuyigwira ndi thandizo lochokera ku bungwe la UN-AIDS kuchokera mdziko la  South Africa.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>