Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ambuye Msusa Ayamikira Akhristu a Parishi ya Bvumbwe

$
0
0

Akhristu a mpingo wakatolika mu arkidayosizi ya Blantyre awayamikira kamba kochilimika pa zampingo wodzidalira pomwe akugwira ntchito za chitukuko m`maparishi awo.  

Arkiepiskopi wa dayosiziyi, Ambuye Thomas Luke Msusa, anena izi pa mwambo wansembe ya misa  yodzodza  adikoni awiri a mu dayosiziyi kukhala ansembe achipani cha Montfort ku parish ya Bvumbwe komanso pomwe parishiyi imakondwerela  nkhoswe yake yomwe ndi Amalitiri Oyera a ku Uganda.

Ambuye Msusa ayamikira  akhristu a Parishiyi omwe amanga  Goloto lokongola pa iwo wokha osadalira  thandizo lakunja zomwe ati zachitika  kamba kakudzipereka kwawo.

“Ndikuthokoza atsogoleri a parishi ino ya Bvumbwe mogwirizana ndi atsogoleri a arkidayosizi chifukwa chotenga dzina la kudzidalira ndi kuliyika m’manja mwanu.

Iwo anayamikira anayamikira akhristuwa kamba kovomera pempho la a Papa chaka chino pamene tikukondwelera chaka cha chifundo,”anatero ambuye Msusa.

Pomaliza Ambuye Msusa alangiza akhristu kuti athandize ansembe omwe adzozedwa kumenewa powapempherera ndi kuwapatsa zosowa zawo.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>