Bungwe la mpingo wakatolika la chilungamo ndi mtendere la Catholic Commission for Justice and Peace (CCJP) ladzudzula aphungu a ku nyumba ya malamulo kamba ka chisankho chomwe ena mwa iwo akuchita chosapita ku nyumbayi ati zomwe ndi kunyozera ufulu wa anthu woyenera kukhala ndi chitukuko.
Yemwe akuyimilira mkulu wa bungweli ku likulu la mpingo wa katolika mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM), a Martin Chiphwanya walankhula izi kudzera mu uthenga omwe bungweli latulutsa potsatira kusapita kwa aphunguwa ku nyumba ya malamulo.
Iwo ati aphunguwa akuyenera kuzindikira kuti anasankhidwa ndi anthu a m’madera omwe amachokera kuti aziwayimilira ku mavuto omwe akukumana nawo.