Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Boma Latsimikiza Kuti Zitukuko Zitha Posachedwa M’boma La Machinga

$
0
0

Anthu a m’madera a mafumu a Chiwalo komanso Kapoloma m’boma la Machinga awatsimikizira kuti zitukuko zomwe zikugwiridwa m’madera awo zifika kumapeto posachedwapa.

Nthandizi wa nduna ya za nyumba ndi malo, a Charles Nkozomba, alankhula izi ndi Radio Maria Malawi poyankhapo ena mwa madandaulo omwe anthu a derali anadandaula kaamba ka kuchedwa kutha kwa zitukuko ngati milatho ndi sukulu.

A Nkozomba ati zitukukozi zachedwa kutha kaamba koti ndalama zogwilira ntchitoyi zikuchokera ku thumba la chitukuko cha mdera la phungu lotchedwa Constituency Development Fund (CDF)zomwe zimaperekedwa pang’onopang’ono.

“Zitukuko zomwe tinagwirizana chaka changothachi ndi zoti timanga zipatala za ana (under 5 clinics) komanso timanga ma milatho. Ntchitoyi yatenga nthawi yaitali kamba koti ndalama zomwe timagwiritsa ntchito za CDF zimabwera moduladula. Ndiye ngati tili ndi zitukuko zingapo ndalama zija timaika uku pang’ono kwinanso pang’ono zimene zimachititsa kuti zitukukozi zizichedwa,” anatero a Mkozomba.

Iwo ati ali ndi chikhulupiliro kuti zitukuko zonse zomwe zinalonjezedwa chaka chikuthachi zikhala zitata masabata awiri akudzawa pamene dongosolo la ndalama latsopano a boma liziyamba.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>