Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Wapepesa Anthu Amene Akhuzidwa Ndi Chiwembu Mdziko la Bangladesh

$
0
0

Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Fransisko wapereka uthenga wa chipepeso kwa anthu omwe akhudzidwa ndi chiwembu chomwe chaphetsa anthu makumi awiri mu mzinda wa Dhaka mdziko la Bangladesh.

Malinga ndi kalata yochokera ku likulu la mpingowu yomwe yasayinidwa ndi mlembi wake Cardinal Pietro Parolin, Papa ndi wokhudzidwa ndi chiwembuchi ndipo wati mchitidwe wa mtunduwu ndi tchimo kwa Mulungu ngakhalenso pa umunthu.

Malipoti a wailesi ya Vatican ati Papa walonjeza kuti awayikiza m’mapemphero achibale onse a anthu omwe aphedwa komanso anthu omwe avulala pa chiwembuchi.

Padakali pano boma la dziko la Bangladesh lakhazikitsa masiku awiri okhudza maliro a anthuwa ndipo malipoti a wailesi ya BBC ati gulu lomwe lachita chiwembuchi si la zigawenga za Islamic Statekoma ndi gulu lina la za uchifwamba lomwe analithamangitsa mdzikolo zaka khumi zapitazo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>