Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Alamulidwa Kukakhala ku Ndende Zaka 10 Kamba Kopereka Mimba kwa Mtsikana Wachichepere

$
0
0

Mwamuna wina wa zaka 18 zakubadwa amulamula kuti akakhale kundende ndikukagwira ntchito ya kalavula gaga kwa zaka khumi (10) kamba kopereka mimba kwa msungwana wa zaka 15 m’boma la Mwanza.

Mneneri wa apolisi m’bomali, a Edwin Kaunda, auza atolankhani a MANA kuti bwalo lamilanduli lachinayi linapeza a Allan Wizzard wolakwa pa mlandu wopereka mimba kwa mwana wang’ono m’mudzi mwa Chikolosa m’bomalo.

Malinga ndi a Kaunda, a Wizzard omwe amakana mlandu wogwilirira msungwanayu anachita chibwenzi ndi msungwanayu pa 5 May chaka chino ndipo ati tsiku lina msungwanayu anasowa pakhomo pa makolo ake zimene zinachititsa kuti makolowo akadandaule kwa a mfumu omwe analamula anthu kuti ayambe kumusaka ndipo anakampeza kunyumba kwa a Wizzard omwe amati msungwanayo ndi mkazi wawo.

A Kaunda ati msungwanayu anamutengera pa chipatala cha boma cha Mwanza komwe anatsimikiza kuti ali ndi mimba ya mwezi umodzi.

A Wizzard amachokera m’mudzi mwa Minjale mfumu yaikulu govati m’boma lomwelo la Mwanza.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>