Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Francisco wati Ntchito za Migodi Zikomere Anthu Okhala Moyandikana ndi Malowa

$
0
0

Mtsogoleri wampingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco,wapempha mayiko kuti adziwonetsetsa kuti ntchito za migodi zomwe zikuchitika mmayiko awo zikuchitika mokomera anthu  onse maka oyandikana ndi malo omwe migodiyo ikuchitikira.

Papa Francisco,wapereka pempholi muuthenga wake omwe atumizira nthumwi zomwe zili kumsonkhano okhudza chitukuko cha migodi ndi zotsatira zake,omwe ukuchitikira ku likulu la mpingowu ku Vatican.

Cholinga cha msonkhanowo omwe wakonzedwa ndi nthambi yowona za chilungamo ndi mtendere kulikulu lampingowu ndi chofuna kuwunika madandaulo omwe anthu okhala mmadera oyandikana ndi migodi amakumana nawo nthawi zonse.

Mmawu ake mkulu owona zamabungwe a mumpingowu kulikululo Kadino Peter Turkson, wati nthawi zambiri ntchito zamigodi zimabweretsa mavuto monga kuwonongeka kwa chilengedwe ndipo ndi pofunika kuti mayiko aziganizira mbali zonse akafuna kuyambitsa ntchitozi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875