Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all 1875 articles
Browse latest View live

Anthu 13 Afa ndi Bomba Mdziko la Somalia

$
0
0

Anthu khumi ndi atatu afa ndipo ena makumi anayi avulala anthu ena ataphulitsa bomba pahotela ina mumzinda wa Mogadishu mdziko la Somalia.

Mtolankhani wa wailesi ya BBC mumzindawo wati chiwembucho ndi chimodzi mwa ziwembu zikuluzikulu zomwe wakhala akuwona mdzikolo.

Gulu lazauchifwamba la Ishabaab lalengeza kuti ilo ndi lomwe lachita chiwembucho.

Ilo lachita zaupanduzo mtsogoleri wadziko la America Barrack Obama,atangomaliza zokambirana ndi mtsogoleri wa dziko la Kenya za mmene angathanire ndi ziwembu zomwe gululo likuchita mmaiko osiyanasiyana.

Pakadali pano dziko la America ladzudzula zamtopola zomwe gululo lachita.


Maepiskopi Mdziko la Ghana Adzudzula za Mchitidwe Wotaya Pathupi

$
0
0

Maepiskopi a mpingo wakatolika mdziko la Ghana akuyembekezeka kukhala ndi msonkhano okambirana vuto la mchitidwe otaya pathupi omwe akuti wakula kwambiri pakati pa atsikana achichepere mdzikolo.

Mmodzi mwa maepiskopi a mpingowu mdzikolo Bishopu  Joseph Afrifah-Agyekum wa dayosizi ya Koforidua wati mchitidweu wafika poyipa kwambiri mdzikolo pomwe ana ngakhale aku pulaimale akutaya pakati pogwiritsa ntchito njira zosiyansiyana.

Bishop Agyekum wati ma Episkopiwa akhala ndi msonkhano okhudza nkhaniyi pofuna kulimbikitsa ufulu okhala ndi moyo omwenso mpingo wakatolika umalimbikitsa nthawi zonse.

Sister Pauline Dambe Achipani cha Teresian Sisters Amwalira

$
0
0

Sister  Pauline Dambe womwe amatumikira  mchipani cha Teresian Sisters mu Archdiocese ya Lilongwe amwalira lachiwiri pa 29 July  2015.

Iwo amachokera m’mudzi mwa a Chilemba ku parish ya Mtendere mdayosisi ya Dedza.

Malinga ndi akulu akulu akuchipani cha Teresian Sisters,Sister  Pauline Dambe anabadwa mchaka cha 1928 ndipo adalowa  m chipanichi mchaka cha 1951.

 Mwambo woika Mmanda thupi la malemuwa uzachitika lachisanu pa 31 July ku Mlale Parish Lilongwe Archdiocese, nthawi ya 10 koloko mamawa.

Mzimu wa malemu Sister Pauline Dambe  uwuse mutendere.

Ambuye Mpundu Akupeza Bwino Atadwala Nthenda ya Kuthamanga Magazi

$
0
0

Episkopi wa dayosizi ya Lusaka mdziko la Zambia Ambuye Telesphore-George Mpundu atuluka mchipatala lachiwiri sabata ino komwe anagonekedwa mdziko la South Africa.

Polankhula ndi atolankhani pabwalo la ndege la Kenneth Kaunda International, Ambuye Mpundu wati tsopano akupeza bwino.

Iwo athokoza anthu akufuna kwabwino kuphatikizapo mtsogoleri wadzikolo Edgar Lungu yemwe analamula kuti Archepiskopiyo akalandire thandizo lapadera ku chipatala cha Milpark mdziko la South Africa.

Ambuye Mpundu analephera kupitiliza kutsogoleri mwambo wa ukaristia masiku apitawa kamba ka vuto la kuthamanga kwa magazi zomwe zinachititsa kuti agonekedwe pa chipatala china mdziko lomwelo la Zambia asadatumiziwe ku chipatala cha Milpark.

Anthu 15 Afa Atagundidwa ndi Lore Mdziko la Mexico

$
0
0

Anthu oposa khumi ndi asanu amwalira, ndipo ena ambiri avulala modetsa nkhawa  pa mdipiti wamapemphero galimoto la mtundu wa lore litawawomba mtawuni ina mdziko la Mexico.

Malipoti a wailesi yampingo wakatolika kulikulu la mpingowu ku Vatican ati ngoziyo yachitika oyendetsa galimotolo atalephera kuyima mumsewu wina omwe anthuwo amagwiritsa ntchito pamdipiti wamapempherowo chifukwa chothamanga kwambiri.

Malipotiwo ati chiwerengero cha anthu omwe amwalira pangoziyi chitha kukwera kwambiri.

Padakali pano apolisi mdzikolo akufunafuna oyendetsa galimotolo yemwe wathawa ngoziyo itangochitika.

Mipingo ndi Zipembedzo Zithetse Mavuto a Kusiyana Mtundu

$
0
0

Mipingo ndi zipembedzo ati zili ndi udindo waukulu othana ndi mavuto omwe amadza pakati pa anthu chifukwa chosiyana mitundu.

Episkopi wa dayosizi ya Sokoto mdziko la Nigeria Ambuye Mathew Hassan Kukah ndi amene anena izi posachedwapa pamwambo okhazikitsa buku lophunzitsa anthu momwe angalimbikitsire umodzi mumpingo ngati ali osiyana mitundu.

Iye wati poyang’anira ziwawa ndi zaupandu zomwe zakhala zikuchitika mu mbiri ya mitundu ya anthu a muno mu Africa chifukwa cha kusiyana  mitundu,kuzindikiritsa anthu a mitundu yonse zaubwino okhalira limodzi, kungathandize kwambiri kuchepetsa mavutowa.

Iye wati vutoli lingathe mipingo itatengaponso mbali yaikulu yophunzitsa anthu zaubwino okhalira limodzi.

Mipingo ndi zipembedzo ati zili ndi udindo waukulu othana ndi mavuto omwe amadza pakati pa anthu chifukwa chosiyana mitundu.

Episkopi wa dayosizi ya Sokoto mdziko la Nigeria Ambuye Mathew Hassan Kukah ndi amene anena izi posachedwapa pamwambo okhazikitsa buku lophunzitsa anthu momwe angalimbikitsire umodzi mumpingo ngati ali osiyana mitundu.

Iye wati poyang’anira ziwawa ndi zaupandu zomwe zakhala zikuchitika mu mbiri ya mitundu ya anthu a muno mu Africa chifukwa cha kusiyana  mitundu,kuzindikiritsa anthu a mitundu yonse zaubwino okhalira limodzi, kungathandize kwambiri kuchepetsa mavutowa.

Iye wati vutoli lingathe mipingo itatengaponso mbali yaikulu yophunzitsa anthu zaubwino okhalira limodzi.

Dziko la Congo-Brazzaville Lisasinthe Malamulo

$
0
0

Zipani zotsutsa boma ndi mabungwe omenyelera ufulu wa anthu mdziko la Congo-Brazzaville, apempha anthu mdzikolo kuti asalole kuti boma lisinthe malamulo oyendetsera dzikolo ndi cholinga chofuna kupereka mpata kwa mtsogoleri wadzikolo kuti ayime kachitatu pachisankho.

Pamene dzikolo likuyembekezeka kuchititsa chisankho cha pulezidenti chaka chamawa,magulu awiriwa lachitatu anali ndi zokambirana pomwe agwirizana kuti asalole ganizo la boma lofuna kusintha malamulowo.

Padakali pano mtsogoleri wa dzikolo Sassou Nguesso sadakambepo chilichonse pankhani yoyima pachisankhocho koma akumbali yotsutsa akukayikira kuti iye akhoza kuyimanso atalamulira kale dzikolo kwa zaka makumi atatu ndi chimodzi.

Izi zikuchitika pamene boma la dzikolo lakhazikitsa komiti yapadera yomwe ithandize pantchito yowunikira malamulo adzikolo.

Ambuye Thomas Luke Msusa Ayamikira Mgwirizano Womwe Ulipo Pakati Pa Atumiki A Mumpingo.

$
0
0

Ark-episkopi wa ark-dayosizi ya Blantyre olemekezeka Ambuye Thomas Luke Msusa ati mgwirizano pakati pa atumiki a Mulungu ndiwofunikira kwambiri pachitukuko cha m’madayosizi komanso mpingo.

Ambuye Msusa omwenso ndiwapampando wabungwe la maepiskopi mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM) komanso episkopi ogwirizira dayosizi ya Zomba ndi omwe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi pomwe wailesiyi imafuna kudziwa momwe ntchito yawo yotumikira madayosizi awiriwa ikuyendera.

Iwo ati mgwirizano omwe ulipo ndi atumiki osiyanasiyana m’madayosizi awiriwa ndi omwe ukuchititsa kuti ntchito yawo yotumikira madayosiziwa ikhale yotheka.

Pamenepa Ambuye Msusa ati akukhulupilira kuti mtsogoleri wampingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco asankha episkopi wa dayosiziyi posachedwapa kuti athandizane nawo potumikira Mulungu.

Patha chaka chimodzi ndi theka tsopano dayosizi ya Zomba ilibe episikopi wake wake, Ambuye Thomas Luke Msusa  omwe anali episikopi wadayosiziyo  atapemphedwa kutumikira mpingowu mu Ark-dayosizi ya Blantyre.

 

 

 


Abwenzi a Radio Maria Malawi Mu Ark-Dayosizi Ya Lilongwe atolera Ndalama Zothandizira Wailesiyi

$
0
0

Bungwe la abwenzi a Radio Maria Malawi mu ark-dayosizi ya Lilongwe lati lipitiliza kupeza njira zosiyanasiyana zomwe zingathandize bungweli kupeza thandizo loyendetsera wailesiyi.

Wachiwiri kwa wapampando mu bungweli mu ark-dayosiziyo a Allan Tsoka anena izi la Mulungu lapitali pamwambo ogulitsa katundu osiyanasiyana omwe bungweli lapeza pofuna kupeza ndalama zoyendetsera wailesiyi womwe unachitikila ku Parishi ya St Patricks ku area 18. 

Iwo ati bungweli lipitiliza kulumikizana ndi anthu mmadera osiyanasiyana pantchito yotolera thandizo loyendetsera wailesiyi pofuna kuti ntchito zake zipite patsogolo.

Mlendo olemekezeka pamwambowuanali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino olemekezeka a Saulosi Chilima.

 Mmawu ake mkulu owona za mapulogalamu ku Radio Maria Malawi Bambo Joseph Kimu anayamikira abwenzi a wailesiyi mu ark-dayosiziyo kaamba kodzipereka pofunafuna njira zomwe zingathandize kupeza thandizo loyendetsera wailesiyi.

Ndipo Mwapadera Bambo kimu ayamikira wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino chifukwa chokhala nawo pamwambowu posayang’anira kuchuluka kwa ntchito zaboma zomwe amayenera kugwira nthawi zonse.

Iwo ati zomwe olemekezeka a Chilima achita zawonetsa chikhulupiliro chomwe ali nacho pa moyo wa uzimu.

 

 

Bambo Joseph Kimu atha zaka 30 akutumikira Mulungu ngati Wansembe.

$
0
0

 Mwambo wa nsembe yamisa wokodwelera kuti bambo Josephy Kimu atha zaka 30 akutumikira ngati wasembe wachitika loweruka ku Sauya m’mboma la Mangochi.

Bambo Joseph Kimu womwenso ndi a  Director a Radio Maria Malawi anathokoza Mulungu powalola kunkhala wansembe ndiponso anathokoza anthu onse amene awanthandiza kudzera mapemphero.

“Ine sindimayembekezera kupanga mwambowu chifukwa ndimayenela kuzapanga pakantha zaka 50, koma Mai anga ndi amene anandipempha kuti ndipange chakachi.”iwo anatero

Iwo anapitiliza ponena kuti cholinga cha chaka chimenechi ndi  chakuti anthu awapempherere kuti ankhale wolimbikira kutumikira Mulungu ngati wansembe komanso ankhale ndi Mtendele wamumtima.

“Ine ndi mboni yaikulu ya chikondi cha Mulungu ndipo ndimakonda komanso ndimafunitsitsa zinthu zitatu izi kupemphera,kulalika komanso kunthandiza osowa .”Anawonjezera motelo Bambo Kimu

Kumwambowu kunafika anthu wosiyanasiyana kumphatikizanso ansembe,masisteli komanso phungu wadelalo wolemekeza Meleka  Chiwondo.

Ambuye Tarcizius Ziyaye Ayamikila Akhristu Pozidalila Kunthandiza Mpingo.

$
0
0

Akhristu a ku parishi ya St Patricks Area 18 mu arkdayosizi ya Lilongwe awayamikira kamba kodzipereka pantchito zachitukuko.

Ark episkopi wa arkdayosizi ya Lilongwe a Ambuye Tarcizius Ziyaye ndi omwe ayamikira akhristuwa Loweruka pomwe amaika mwala wamadziko pamalo omwe parishiyi ikufuna  imangepo ma ofesi ake.

Iwo ati mpofunika kuti akhristu ayambe kuchitapo kanthu pa nkhani ya mpingo odzidalira ngakhale atapeza thandizo kuchokera kwa ena.

“Ine ndili wokondwa kwambili kuti akhristu aku St Patricks akumanga ma ofesi awo ndipo zikusonyedza kuti akhristuwa amvetsa udindo wawo ndiponso umwini wa mpingo chifukwa mpingo ndi ife tonse ”.Ambuye  Ziyaye anatelo

Ndipo iwo alimbikitsa akhristuwa kuti  kuno ku Malawi Mpingo wa katolika tingathe kuyendetsa tonkha chifukwa sikuti ndife osaukitsisa.

“Munthu ukayesesa kuzidalira umakodwera kuti ntchito waigwira wenkha osati ena akuchitira  zimenezo ndiponso pamene tigwira ntchito yozidalira chinthu chimene tachita, nyumba yomwe taimanga timaisamalira kwambiri chifukwa chinthu tachivutikira”anawonjezera motelo Ambuye Ziyaye

“Unthenga umenewu wakuzidalira ufikire tonse mu Mpingo wanthu M’dziko lanthu kuti ifenso tingathe kuzidalira chifukwa tikamati ayi sitingathe sitizathadi ndipo sitizatukuka.”Ambuye Ziyaye anapitiliza motelo

Tchito yomanga  ma ofesi ku parishiyi ikuyembekezeka kuyamba posachedwapa.

Anthu achiwembu ampha Mkulu wonthandizira Pulezideti wa dziko la Burundi.

$
0
0

Mmodzi mwa akuluakulu othandizira mtsogoleri wadziko la Burundi Pierre Nkuruzinza,waphedwa ndi anthu achiwembu mumzinda wa Bujumbura omwe ndi likulu la dzikolo.

Mkuluyo General Adolphe Nshimirimana, anali mkulu wakale wa asilikali komanso wa nthambi ya ukazitape mdzikolo.Kusowa kwa chitetezo chokwanira kukupitilira mdziko la Burundi kuyambira pomwe mtsogoleri wa dzikolo adalengeza kuti apikisana nawo kachitatu pachisankho cha pulezidenti kufikira pano pamene watenganso udindowu mwezi watha.

Iye wapambana paudindowu pachisankho chomwe zipani zotsutsa boma zidakana kutenga nawo mbali ponena kuti iye adaphwa malamulo adzikolo poyimanso kachitatu atalamulira kale dzikolo kawiri.

Koma pulezidenti Nkuruzinza wati iye amayenera kuyimanso kamba koti  kumayambiliro a ulamuliro wake adachita kusankhidwa ndi aphungu akunyumba yamalamulo pambuyo pankhondo yapachiweniweni yomwe inachitika Mdzikolo.

Bungwe la ECM linkhazikitsa kalata ya Apapa yonkhuzana ndi Zanyengo

$
0
0

Mpingo wakatolika mdziko muno lachiwiri ukhazikitsa kalata yomwe mtsogoleri wa mpingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco, walemba pankhani yokhudza chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo la Laudato Si.

Polankhula ndi Radio Maria Malawi, mlembi wamkulu wabungwe la maepiskopi mdziko muno la Episcopal Conference of Malawi (ECM) Bambo Henry Saindi ati maepisikopi mdziko muno aganiza zokhazikitsa kalatayi mdziko muno poyang’anira mfundo zomwe zili mkalatayi zomwenso zikukhudza kwambiri dziko lino.

Iwo ati kalata yomwe Papa Francisco walemba ndi pempho lalikulu kwa anthu padziko lonse lapansi kuti akhale ndi udindo osamalira zachilengedwe potengera momwe kuwonongeka kwa chilengedwe kukukhudzira anthu.

“ifeyo ngati mpingo kuno ku Malawi takoza mwambo woti kalata ya Apapa francisco ya Laudato si  yonkhuzana ndikusintha kwa nyengo ikhazikitsidwe kuno ku Malawi ”

Iwo anati chimene chapangisa kuti pabwele ganizoloti ankhazikitse kalata ya Apapa ndi chifukwa choti Malawi wankhuzidwa ndikusintha kwa nyengo  mzaka zimenezi.

“ife tikuwona kuti kalata ya Apapa yonkhuza chilengedwe ndimwayi chifukwa choti ikupereka mayankho kumavuto womwe dziko la Malawi lankhala likukumana nawo, anthu ambiri nyumba zawo zinangwa chifukwa chama floods amene analipo, minda, mbewu zomwe adabyala  zinakokoloka.” Bambo Henre Saindi anatelo

“Ma episcope anthu aganiza zonkhazikitsa kalata yomweyi     ya apapa kuti unthenga womwe Apapa alemba mu kalata yayo owapatsa anthu udindo wosamalila chilengedwe m’dziko lomwe akunkhala   ufike kwa wina aliyense” anawonjezera motelo Bambo Henry Saindi

 Mwambo onkhazitsa kalatayi kuno ku Malawi uchitika ku Bingu International Conference Center M’dzinda wa Lilongwe.

Mtsikana wa Zaka 15 Wamwalira Chigayo Chitamdula Mutu.

$
0
0

Mwambo woyika m’manda thupi la Msungwana wina wa zaka khumi ndi zisanu zakubadwa amene wamwalira chitsulo cha Chigayo chitamudula mutu M’boma la Ntchisi wachitika lolemba m’bomalo.

Ngoziyi inachitika lolemba sabata ino pomwe msungwanayu anapita kuchigayo  ndi cholinga choti akakonoletse mphale limodzi ndi azake.

Wofalitsa nkhani za apolisi ku mtchisi Sargent Gredisoni Bumpha   anati Mtsikanayo malemu Bertha Khisi anavala chitenge khosi mwake ndiye anayandikana  ndi mtondo wachigayocho zomwe zinapangisa kuti chitenje chomwe chinali khosi mwake muja chikolane  ndi chitsulo chomwe chinayamba kupukusa Mutu wake  ndipo Mutu watsikanayo unaduka popo.

Ngoziyi inachitika pachigayo cha a Gwaza ndipo Malemuyu amachokera mmudzi mwa  Chinkhugwa  mfumu yaikulu Kalomo mmbomalo.

Bungwe la ECM Lankhazikitsa Kalata ya Apapa Yonkhuzana ndi Zanyengo

$
0
0

Mpingo wakatolika mdziko muno dzulo wankhazikitsa kalata yomwe mtsogoleri wa mpingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco walemba pankhani yokhudza chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo la Laudato Si.

Mwambowu womwe unachitikira ku Capital Hotel unakhazikitsidwa ndi Ambuye Thomas Msusa koma yemwe anatsogolera mwambowu anali mlembi wa bungwe la Episcope Conference Of Malawi (ECP)Bambo Henry Saindi

Ambuye Thomas Msusa anati pofunika kwambiri kuti chilengedwe chitetedzedwe popangira mbado wammawa.

Cholinga cha mwambowu  kunali kupeza njira zonthanilana ndi mavuto akusitha kwa nyengo.

“Pafunika kuti ku Malawi kuno kukhazikitsidwile njira zonthanilana ndi kusintha kwa nyengo,ndipo pamafunika kuti bugwe la National Disaster Management lizithandizidwa ndi ndalama zokwanila pofuna kunthana ndi ngozi zobwera kamba kakusintha kwa nyengo”. Ambuye Msusa anatero.    

Ndipo nduna yowona zachilengedwe ndi migodi wolemekezeka a Bright Msaka inati ntchito yolimbana ndi kusintha kwa nyengo mdziko muno ndiyofunika kugwilana manja chifukwa boma palonkha silingakwanitse.

Iwo anawonjezera ponena kuti anthu akuyenera kumasamalira chilengedwe chimene Mulungu anatisiira osati kumachiwononga ayi.

Pamwambowu panawelegwedwa buku limene limakamba udindo wa anthu wosamalira chilengedwe.  


Papa Francisco Ayamikira Ana Wotumikira pa Misa.

$
0
0

Mtsogoleri wa mpingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco wayamikira ana othandizira misa pa guwa kaamba kodzipereka pa ntchito yawo.

Papa Francisco wanena izi dzulo kulikulu la mpingowu ku Vatican pamsonkhano wa chisanu ndi chinai wa ana otumikira paguwa omwe anachokera mmaiko osiyanasiyana.

Iye wati kutumikira mmiyambo ya Misa  pa guwa komwe anawa amachita kumawathandiza kukhala pafupi ndi Yesu Khristu kudzera musacramenti ya Ukarisitiya.

Papa Francisco Apaleka Mwayi woti Anthu Azawona Thupi la Malemu Padre Piyo

$
0
0

Likulu lampingo wakatolika lalengeza kuti thupi la malemu Piyo oyera yemwe amadziwika bwino ndi dzina loti Padre Pio  adzalitulutsa mmanda kuti anthu adzakhale ndi mwai opereka ulemu kwa iye kuyambira pa 8 mpaka pa 14 February 2016.

Papa Francisco ndi yemwe waganiza zopereka mwai kwa anthu oti adzapereke ulemu wawo kwa Padre Pio ndipo pali chiyembekezo choti thupi lake lidzakhalaponso pamwambo wa phulusa wachaka cha mawa mtchalitchi lalikulu la St Peters Basilica pomwenso mpingo udzakhale ukukondwelera chaka cha chifundo cha Mulungu.

Likululi lati kupezeka kwa thupi la Pio Oyera panthawiyi chidzakhala chinthu chamtengo wapatali kwa atumiki a Mulungu pomwe adzalimbikitsidwe kudzipereka pautumiki wawo monga momwe Padre Pio adachitira.

Nyamata Wazaka 19 Ampeza Wolakwa Pamulandu Wogwililira.

$
0
0

Bwalo lamilandu m’boma la Dowa, lalamula m’nyamata wa zaka 19 zakubadwa kuti akagwire ukaidi kwa zaka zisanu ndi zinai kamba komupeza olakwa pa mulandu ogwililira msungwana wazaka khumi ndi zinai.

Mnyamatayo Velemo Handison anawuza bwalolo kuti zomwe anachitazo zinali zogwirizana ndi msungwanayo.

First Grade Magistrate Amulani Phiri anati  mnyamatayo, ndiwolakwabe ngakhale zikanakhala  zogwirizana kamba koti Msungwanayo ndi mwana woti sangathe kupanga chiganizo choyenera chifukwa ndiwosakhwima mmaganizo.

Iye ndi wammudzi mwa Chiguduli mdera la mfumu yayikulu Msakambewa m’boma lomwelo la Dowa.

Zomba Dayosizi Ikonza Mwambo Wokumbukira Umoyo wa Ana.

$
0
0

Bungwe la zaumoyo mu mpingo wa katolika mu Dayosizi  ya Zomba linakonza tsiku lokumbukira za umoyo  wa ana mu Dayosiziyi.

Mwambowu unachitikira m’mudzi mwa Moto m’dera  la mfumu yaikulu  Mulumbe m’boma la Zomba ndipo mutu watsikuli unali wakuti ‘Mwana aliyense ali ndi ufulu wolandira thandizo la zaumoyo’.

  Mkulu oyang’anira za ana ku bungweli Mai Lucia Maele anati  mwambowu umene ndiwofunika kwambiri chifukwa mwana wathadzi yenkha ndi amene angapite ku sukulu posatengera kuti ngolumala kapena ayi.

“Mwambowu tinakoza kuti uchitikire kuno ku Zomba kwachinseu   makamaka kuchingale  chifukwa chakuti dela limeneli lili kutali ndi zipatala ndiye Makolo ambiri amalemphera kutenga  ana awo kupita nawo kuchipatala mapeto ake ana amakula monyentchela ”anatelo Mayi Maele.

 Iwo anawonjezera ponena kuti kumwambowu ana anakwera sikelo,kulandira katemela komanso kuyezedwa Malungo komanso ananthandiza  ana amene ali  aalubino,matenda apankhungu, komanso Maso.  

Kumwambowu makolo anapatsidwanso mwayi woyesetsa magazi komanso kuthamanga kwamagazi.

Bungwe la ECM Lakhazikitsa Kalata ya Apapa Yonkhuzana ndi Zanyengo

$
0
0

Mpingo wakatolika mdziko muno dzulo wakhazikitsa kalata yomwe mtsogoleri wa mpingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco walemba pankhani yokhudza chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo la Laudato Si.

Mwambowu womwe unachitikira ku Capital Hotel unakhazikitsidwa ndi Ambuye Thomas Msusa koma yemwe anatsogolera mwambowu anali mlembi wa bungwe la Episcope Conference Of Malawi (ECP)Bambo Henry Saindi

Ambuye Thomas Msusa anati pofunika kwambiri kuti chilengedwe chitetedzedwe popangira mbado wammawa.

Cholinga cha mwambowu  kunali kupeza njira zonthanilana ndi mavuto akusitha kwa nyengo.

“Pafunika kuti ku Malawi kuno kukhazikitsidwile njira zonthanilana ndi kusintha kwa nyengo,ndipo pamafunika kuti bugwe la National Disaster Management lizithandizidwa ndi ndalama zokwanila pofuna kunthana ndi ngozi zobwera kamba kakusintha kwa nyengo”. Ambuye Msusa anatero.    

Ndipo nduna yowona zachilengedwe ndi migodi wolemekezeka a Bright Msaka inati ntchito yolimbana ndi kusintha kwa nyengo mdziko muno ndiyofunika kugwilana manja chifukwa boma palonkha silingakwanitse.

Iwo anawonjezera ponena kuti anthu akuyenera kumasamalira chilengedwe chimene Mulungu anatisiira osati kumachiwononga ayi.

Pamwambowu panawelegwedwa buku limene limakamba udindo wa anthu wosamalira chilengedwe.  

Viewing all 1875 articles
Browse latest View live


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>