Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Chipatala cha Praises Chikupereka Thandizo Laulere

$
0
0

Chipatala cha Praises chati chakonza dongosolo lopeleka thandizo lina la zachipatala mwaulele pofuna kuthandiza anthu a m’dera lomwe kuli chipatalachi.

Mkulu wa chipatalachi Dr. Nelson Munthali wanena izi pokondwerera kuti chipatalachi chakwanitsa zaka khumi ndi zisanu (15) chikuthandiza anthu a m’dera la Machinjiri mu m’dzinda wa Blantyre.

“Tinatsegula chipatalachi pa 1 august 2001ndiye tawona kuti pamene tafikapa anthu a kuno ku machinjiri akhala akutipanga support mu zinthu zambiri mpaka chipatalachi chakula ndiye tawona kuti tiwabwerenso anthu a dera lino chifukwa cha ubwino wawo. Pachifukwa chimenechi kuyambira pa 1 august anthu onse ochokera kuno kuno kumachinjiri samalipila ndalama yokawonana ndi a dotolo komanso pa ndalama ya treatment yawo tizichotsako 20 kwacha pa 100 kwacha iliyonse. Komanso anthu amene azichokera kutalibe tiziwabwezera transport,” anatero a Munthali.

Iwo anati apitirizane kuthandiza anthu kudzera mu ntchito za chipatala pozindikira kuti munthu amene amakhala mtauni amayenera akhale wathanzi kuti athe kugwira ntchito yake moyenera.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>