Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mzika ya Dziko la DRC Yafa Itamwa Mowa Osadyera M’boma la Dowa

$
0
0

Mzika ina ya dziko la Democratic Republic of Congo (DRC), yafa itamwa mowa osadyera  kumalo osungirako anthu othawa kwawo a Dzaleka m`boma la Dowa.

Wofalitsa nkhani za apolisi m`boma la DowaSergent Richard Kaponda  watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati mamunayu ndi Kimongo Kalambo  wazaka 37 zakubadwa  ndipo amakhala yekha kunyumba kwake pamsasawu.

Malinga ndi abale ake,  mkuluyu anachoka ndikupita kumalo ena omwera mowa komwe anakhalako masiku atatu akumwa opanda kudya chakudya.

Mneneri wa apolisiyu wali lipoti lakuchipatala lasonyeza kuti mkuluyu wafa kaamba komwa mowa osadyera.  Mkuluyu amachokera m`dera la South Kivu m`dziko la DRC.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>