Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apezeka ndi Minyanga ya Njovu

$
0
0

Apolisi munzinda wa Lilongwe amanga mwamuna wina wazaka 27 atampeza ndi minyanga ya njovu.

Malinga ndi wofalitsa nkhani za apolisi munzindawu, Inspector Kingsley Dandaula,   mkuluyi Ackim Bwanali amasunga minyangayi m`galimoto lake pamalo otsukira magalimoto ku Falls Estate munzindawu.

Ndipo apolisi mogwirizana ndi ogwira ntchito kumalo osungirako nyama zachilengedwe anafika pamalowa ndikupeza minyangayi m`galimotolo.

Mamunayu amachokera m`mudzi mwa Talirani kwa mfumu yaikulu Chowe m`boma la Mangochi. Apolisi  apempha anthu m`dziko muno kuti adzikanena kupolisi ngati akudziwa kuti pali anthu ena omwe ali ndi minyanga yanjovu.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>