Apolisi munzinda wa Lilongwe amanga mwamuna wina wazaka 27 atampeza ndi nyanga za njovu.
Malinga ndi wofalitsa nkhani za apolisi munzindawu, Inspector Kingsley Dandaula, mkuluyi Ackim Bwanali amasunga nyangazi m`galimoto lake pamalo otsukira magalimoto ku Falls Estate munzindawu.
Ndipo apolisi mogwirizana ndi ogwira ntchito kumalo osungirako nyama zachilengedwe anafika pamalowa ndikupeza nyangazi m`galimotolo.
Mamunayu amachokera m`mudzi mwa Talirani kwa mfumu yaikulu Chowe m`boma la Mangochi.
Apolisi apempha anthu m`dziko muno kuti adzikanena kupolisi ngati akudziwa kuti pali anthu ena omwe ali ndi nyanga za njovu.