Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Francisco Alimbikitsa Ansembe Kuthandiza Akhristu pa Mavuto

$
0
0

M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse PapaFrancisco walimbikitsa ansembe mu mpingowu kuti azikhala okhudzidwa ndi kuthandiza pa mavuto omwe akhristu akukumana nawo.

Papa wati ansembe akuyenera kuwonetsa zitsanzo zabwino kamba koti mulungu anawapatula kuti akhale abusa oweta nkhosa zake  osati akapitawo , kapena kuti akulu a oweluza milandu, choncho zochita zawo zikuyenera kusonyezadi mtima wa chikondi pakati pa omwe amawatumikira.

Papa Francisco anapeleka uthengawu lachisanu, pomwe amachititsa nsembe ya ukaristia pa tchalichi lina ku likulu la mpingowu ku Vatican.

Iye anadzudzula ansembe omwe samawonetsa chidwi chotenga nawo mbali pa ntchito zosiyanasiyana zochitika mu mpingowu.

Pambombowu panachitikanso chaka chokondwelera kuti Cardinal Javier Lozano Barragan wakwanitsa zaka 60 akutumikira Mulungu ngati wansembe mu mpingo wakatolika .


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>