Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha anthu akufuna kwabwino kuti agwirane manja pofuna kuthetsa umphawi pokhazikitsa malamulo othandiza mabanja komanso kupereka mwai wa ntchito kwa anthu.
Papa amalankhula izi ku likulu la mpingowu ku Vatican pomwe lero dziko lonse likuchita tsiku loganizira kuthetsa umphawi.
Malipoti a wailesi ya Vatican ati Papa wapempha anthu omwe anasonkhana pa bwalo la tchalitchi la St. Peter’s kuti akuyenera kupemphera kosalekeza komanso azipemphelera mtendere.