Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

ANTHU OKWIYA AVULAZA ABALE A MFUMU KU NTCHISI

$
0
0

Anthu ena ozungulira dera la mfumu Chikho mboma la Ntchisi avulaza abale a mfumu ya deralo komanso kuwononga katundu wa ndalama zoposa 117 thousand pokwiya ndi ulamuliro wa mfumuyo.

Mneneli wa apolisi mbomalo seagent Gladson M’bumpha watsimikiza za nkhaniyi. A M’bumpha ati anthuwo anatsogoleredwa ndi a Ziyendammanja Chunga, Kapalamula Nkhoza komanso a Kankhulukute Mapulanga.

“Chomwe tingapemphe mtundu wa a Malawi ndichoti  ngati pali vuto pa nkhani za ufumu ndi bwino kupita kwa bwanankubwa wa bomalo osati kupanga zipolowe”, atero a M’bumpha.

Pakadali pano apolisi akuti ali mkati mofufuza kuti agwire anthu omwe akukhudzidwa kuti akayakhe milandu yowononga katundu komanso kuvulaza anthuwo.

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>