Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apolisi 6 Aphedwa mu Mzinda wa Kirkuk Mdziko la Iraq

$
0
0

Apolisi asanu ndi m’modzi 6 komanso anthu ena 16 afa pa chiwembu chomwe gulu la za uchifwamba la Islamic state lachita pa nyumba za boma mu mzinda wa Kirkuk mdziko la Iraq.

Malipoti a wailesi ya BBC ati asilikali a gulu la Islamic state okwana khumi ndi awiri 12 aphedwanso.

Malipoti ati izi zikuchitika pamenenso kumenyana kwa asilkali a dzikolo ndi zigawengazi mdera la Mosul kukupitilira pamene asilikali a dzikolo akufuna kulanda deralo m’manja mwa zigawengazi.

Mapemphero a tsiku la lero lachisanu alephereka mdzikolo kaamba koti mizikiti yonse ndi yotseka kaamba koopa  kuchitidwa chiwembu ndi zigawengazi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko