Akaidi oposa 1 hundred 70 athawa mu ndende ina kumpoto kwa dziko la Haiti.
Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC, akaidi omwe athawawo ati aba mfuti zisanu ndi kupha mulonda m’modzi wa pa malowa komanso mkaidi wina.
Malipoti ati akaidi awiri avulazidwa pa kumenyana komwe kunabuka pakati pa akaidiwa ndi alonda apa malowa.
Padakali pano pamene ntchito yoyang’ana akaidiwiwa ili mkati, bungwe la United Nations UNlagwira akaidi khumi ndi m’modzi 11 koma pali chioopsezo choti akaidi ena sakwanitsa kuwagwira kaamba koti akaidi apa ndendeyi ati samavala unifolomu.