Kusowa kwa masomphenya a zipani zandale zosiyanasiyana mdziko muno akuti ndi komwe kukuchititsa atsogoleri azipani zina kusakhazikika mu chipani chimodzi.
Mtsogoleri wa chipani chotsutsa boma cha Umodzi, Professor John Chisi wanena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi.
Proffesor Chisi wanena izi kutsatira kuchoka kwa akuluakulu ena mzipani zawo zandale omwe alowa mu chipani cholamula cha DemocraticProgressive (DPP) zomwe malinga ndi a Chisikumeneku nkusowa masomphenya komanso masanje pa nkhani za ndale mdziko muno.