Achinyamata a bungwe la Young Christian Workers (YCW) mumpingo wa katolika awalangiza kuti azigwiritsa bwino ntchito maluso atsopano omwe akubwera mdziko muno monga ma computer komanso internet pantchito yofalitsa mawu a Mulungukomanso kupezapo zinthu zokhuza maphunziro.
Bambo mfumu a parish ya Kadikira, Bambo Godferry Ntchera anena izi pa m`bindikiro watsiku limodzi wa achinyamata a YCW a dinale ya Limbe omwe unachitikira ku NantipwiriPastrol Centre.
“Tikuwunikikira za utumiki wa achinyamata ngati mboni za Yesu Khristu m’masiku amakono ano. Cholinga ndi chakuti achinyamata ngakhale akumana ndi mavuto osiyanasiyana asafooke kapena kubwelera mmbuyo koma akhale ndi mtima opitiriza kutumikira. Iwowanso awathandize anzawo omwe sachita zachikhristu kuti atembenuke mtima ayambenso nawo kukhala mboni za Yesu Khristu chifukwa achinyamatawa ndi mchere komanso kuwala kowalira ena amene ali mu mdima,” anatero bamboo Ntchera.
Iwo ati achinyamata akusokonekera kamba koti akumaonera zinthu zolaula ndi makhalidwe olakwika zomwe pamapeto pake zikumasokoneza moyo wawo wanthupi ndi wauzimu.
M`mawu ake wapampando wa bungwe la YCWmudinaleyi LenardMataka wati kudzera mu m`bindikirowu achinyamata alimbikitsidwa zomwe ziwathandize kuthana ndi mavuto omwe amakumana nawo tsiku ndi tsiku komanso kukhala nyale za ena.