Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ophunzira a YCS Akhale Owonetsa Makhalidwe Abwino-Bambo Mwakhwawa

$
0
0

Ophunzira a mpingo wa katolika msukulu za sekondale mdziko muno awapempha kuti akhale owonetsa makhalidwe abwino.

Mkulu wa ku ofesi yoona za utumiki wa apapa ya Pontifical Missionary Societies (PMS) ku likulu la mpingo wa katolika mdziko muno ku Episcopal Conference of Malawi (ECM) bambo Vincent Mwakhwawa anena izi pambuyo pa msonkhano wa masiku awiri wa bungwe la ophunzira achikatolika msukulu za sekondale la Young Christian Students (YCS) omwe unachitikira ku Our Lady of Africa mu arkidayosizi ya Lilongwe.

Iwo ati ophunzirawa akuyenera kukhala akhristu olimba popereka uthenga wabwino wa yesu khristu kwa anzawo ndi kutsata komanso kuwonetsa moyo wa chikatolika paliponse pomwe akhala.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>