M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wagwirana manja ndi bungwe la ma Episkopi a mpingo wakatolika m’dziko la Brazilpa ntchito yobwezeretsa chilengedwe.
Papa wati mpingo m’dzikoli umatenganso mbali yaikulu yosamalira chilengedwe ndi anthu osowa.
Iye anati kuwonongeka kwa chilengedwe ndi vuto lalikulu lomwe lakhudza mayiko padziko lonse.
Dziko la Brazil ati ndi limodzi mwa maiko omwe lili ndi nthaka yabwino ndipo inagawidwa m’magulu asanu ndi limodzi (6).