Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apolisi Amanga Anthu 20 ku Mchinji

$
0
0

Anthu makumi awiri (20) ali m’manja mwa apolisi m’boma la Ntchisi kaamba kowaganizira kuti apalamula milandu yosiyanasiyana.

Malingana ndi wofalitsa nkhani za apolisi m’bomalo,  Sergeant Gladson Mbumpha, anthu-wa awagwira mu sabata-yi, apolisi atakhwimitsa chitetedzo m’madera ena, monga pa msika wa pa boma, ndi wa khuwi m’bomalo.

Yemwe amatsogolera ntchito-yi ndi Detective Superintendent Getrude Mnkhondia. Iwo ati anthu-wa ndi a zaka zapakati pa 20ndi 45.

Malingana ndi a M’bumpha ina mwa milandu yomwe anthu-wa akuyenera kukayankha ku bwalo la milandu ndi yotsekula malo omwera mowa nthawi yosavomelezeka, kuchita za malonda opanda ziphatso zowayeneleza, yakuba, yogwilira ndi ina yambiri.

Padakalipano anthu-wa ali m’manja mwa apolisi ndipo akaonekera ku khoti posachedwa. 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>