Apolisi m’boma la m’boma laDowaakufunafuna dalaivala wa galimoto ina kamba komuganizira kuti anagunda ndi kupha a Akimu Dayison a zaka 38zakubadwa m’bomalo.
Ofalitsa nkhani za apolisi m’bomalo Sergeant Richard Kaponda ngoziyi yachitika usiku wapa 8 mwezi uno pomwe dalaivalayu anaomba bambo-yu mu msewu Salima kupita ku Lilongwe. Ngozi-yi inachitikira m’mudzi mwa Sole m’bomalo.
A Kaponda ati dalayivala wa galimoto lomwe linaomba ndi kupha malemu-wa atachita ngoziyo akuti anathawa ndipo apolisi akhadzikitsa ntchito yosakasaka ndalaivala-yu.
Malemu-yi Akimu Dayson anali wochokera m’mudzi mwa Singo m’dera la mfumu yayikulu Mkukula m’boma lomwelo la Dowa.