Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Francisco Atsindika Zakufunika Kolankhula Mwa ufulu.

$
0
0

M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse papa Francisco wauza ma episikopi a mpingowu m’dziko la Italy kuti ndi bwino kulankhula mwa ufulu ngakhale zolankhulazo zitakhala kuti sizingakondweretse aliyense.

Papa Francisco amalankhula izi ku likulu la mpingo-wu potsekulira msonkhano wa nambala 70 wa ma episikopi a mpingowu a m’dzikomo.

Iye wati amakhulupilira kuti kulankhula mwachilungamo kumathandiza kaamba koti anthu sakhala ndi mpata wolankhulanso za miseche.

Polankhula wapampando wa bungwe la ma episikopili m’dzikomo Cardinal Angelo Bagnasco wapempha ma episikopi-wa  kuti adzipereke pa ntchito zokweza bungwe-li.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko