Chipani chotsutsa boma cha Umodzi chati sichikuonapo kulakwikwa kuli konse pa nkhani yoti alimi adzigulitsa chimanga chawo kwa Mavenda.
Mtsogoleri wachipanichi PROFESSOR JOHN CHISI ndi amene wanena izi pofotokozera RADIO MARIA MALAWI. Iwo ati, a Malawi akugulitsa chimanga chawo kwa mavenda kaamba koti alibe njira ina yoti ndikupezera ndalama kaamba kakusowa kwa ntchito mdziko muno. PROFESSOR CHISI anati ma venda ndi anthu amene angathe kukhala ndi nthawi yabwino yosamalira chimanga ngati angagule chisanaumitsitse. Pamenepa PROFESSOR CHISI anayamikira boma posafulumira kugula chimanga kudzera mu misika ya ADMARC kaamba koti ndichosaumitsitsa zomwe ati chikhoza kukaonongeka.