Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Likulu la Mpingo Wakatolika pa Dziko Lonse Liyamikira Dziko la Malawi

$
0
0

Akhristu a mpingo wakatolika m’dziko muno awayamikira kamba kopeleka molowa manja m’miyambo yonse yomwe mpingowu umakhala ukupempha thandizo kuchokera kwa iwo.

Likulu la mpingowu ku Rome m’dziko la Italy , kudzera  mwa m’tsogoleri wa mpingowu padziko lonse Papa Francisco  ndi lomwe lanena izi kudzera m’chikalata chomwe latumizira mpingowu m’dziko muno , chomwe kwambiri chili ndi uthenga wothokoza akhristu a mpingowu m’dziko muno kamba kopeleka mowolowa manja mu zopeleka zawo chaka chatha.

Malingana ndi mkulu  ku ofesi yoona za utumiki wa a papa m’dziko muno ya Pontifical Mission  Societies (PMS) yomwe ikupezeka ku likulu la mpingowu ku Episcopal Conference of Malawi (ECM) Bambo Vincent Mwakhwawa, mpingo wakatolika m’dziko muno unapeleka ndalama zokwanira 25 million kwacha , zomwe ndi zambiri kusiyana ndi momwe mpingowu wakhala akukupelekera zaka za m’buyomu.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>