Akhristu a mpingo wakatolika m’dziko muno awalimbikitsa kuti azikonda kulemekeza Sacrament la Ukaristia kamba koti sacramentili ndi limodzi mwa ma sacrament opamba pakati pa akhristu mu mpingowu.
Bambo Edwin Lambulira , omwe amatumikira mu Parish ya Kausi mu dayosi ya Mangochi , ndi omwe anena izi pomwe amatsogolera mwambo wopeleka sacramentili koyamba kwa akhristu ena ampingo-wu.
Bambo Lambulira alangiza akhristu omwe ayamba kulandira sacramenti-li mu parishi-yi kuti adzikonda kumadziyeletsa polapa zakwayipa zawo , ndi kuti pomwe akulandira sacramenti-li adzikhala ali anthu oyera mitima, zomwenso zimathandiza kumanga ubale wabwino ndi mulungu.
Mwambo-wu unachitikira ku tchalichi la St John yomwe ndi nthambi ya parish ya Kausi mu dayosiziyi.