Anthu a m’madera a mmaboma a Zomba, Machinga ndi Blantyre ati ndiokondwa kaamba ka kubwera kwa komiti yowona za misewu ya kunyumba ya malamulo yomwe inakayendera msewu wa Chingale umene wadutsira m’ma boma-wa.
Polankhula ndi Radio Maria Malawi wapampando wa comiti-yi a Victor Mbewe ati kimiti yawo inadzayendera msewuwu kamba kokhudzidwa ndi mavuto omwe anthu akupitilira kukomana nawo pa nkhani zokhudza mayendedwe.
Iwo ati komiti yawo iyesetsa kuti msewuwu ukonzedwe mwa changu.
Ena mwa amene anapezekanso pa mkumano woyendera maderawa ndi monga a episikopi a mpingo wakatolika mu dayosizi ya Zomba , ambuye George Tambala, Bambo Henery Saindi omwe ndi mlembi wa mkulu wa bungwe la ma episikopi a mpingo wakatolika m’dziko muno ku ECM , komanso bambo Peter Mlomole omwe amaona zachitukuko mu dayosizi ya Zomba.